Thu. May 2nd, 2024

Chisa Isangalala ndi anthu aku Chikwawa

By: Felix Van Captain Oggess

Anthu okhala mmudzi wa Biyala kwa mfumu yayikulu Ngabu ku Chikwawa apephedwa kuonetsa chikondi komanso kukhala bwino ndi anzawo mu nyengo ino yomwe a khirisitu amakumbukira infa komanso kuuka kwa Ambuye Yesu Khirisitu.

Mkulu wa sukulu ya nkombaphala ya Chisa, a Michael Ndelemani ndi omwe anayakhula izi pomwe sukuluyi mogwirizana ndi anthu ena imasangalala nyengo ya kuuka kwa ambuye Yesu khirisitu mmudzi mwa Biyala mbomali.

Iwo anati ndikofunika kuti anthu alingalire za chikondi chomwe Yesu anationetsera ndipo akhale achikondi kwa anzawo pofunirana mafuno abwino. Powonjezera apo a Ndelemani anati sukulu ya Chisa inachiona cha nzeru kuti pomwe ikupereka maphunziro a nkombaphala kwa ana ang`ono angawanenso mawu opatsa moyo ndi makolo omwe amalera anawa.

Poyakhulapo a Enock Biyala omwe ndi mfumu ya mudziwu anati ndi osangalala ndi zomwe sukulu ya Chisa yapanga ponena kuti izi zapangitsa anthu ochuluka kubwera pamodzi kudzanva mawu a chauta zomwe zipangitse kuti pakhale kudalirana pamene akugwira tchito zosiyasiyana za chitukuko.

Mwazina ku mwambowu kunali ubatizo, kudyera pamodzi, kugawana mawu a Mulungu, Kuvina, masewero a mpira komanso kuonera kanena wa masautso a Yesu Khirisitu.

Kupatula kupereka maphunziro kwa ana a nkombaphala, sukulu ya Chisa imaphunzitsanso amayi maluso osiyanasiyana kuti akhale odzidalira komanso kugwira ntchito ndi achinyamata madera a kumidzi.

Sukulu ya mkombaphala ya ulere ya Chisa inatsekulidwa m`chaka cha 2018 pofuna kuchepetsa mavuto omwe ana okhala madera akumidzi amakumana nawo. Sukuluyi ikupezeka maboma a Chiradzulu, Balaka komanso Chikwawa.

Related Posts

David Bisnowaty Israeli-Born Malawi Parliament Member: Actions, Not Words, Will Change Africa for the Better

Malawi MP David Bisnowaty. How does the Israeli-born son of an eastern European Holocaust survivor end up as a parliament Read more

David Bisnowaty former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country

Political cum and former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country https://youtu.be/S20UYlVcHs8

AGHF Feeds Patients, Guardians At Mangochi District Hospital

A giving hand foundation is a local organisation working in various programs in Malawi. On Thursday the organization together with Read more

The British NCA Operations In Malawi Remain Questionable, Britons Aim To Topple Tonse Government

Exposed! British NCA bankrolls PIJ to victimize successful business persons, politicians, judges in Malawi The truth be told! The establishment Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window