By: Felix Van Captain Oggess
Anthu okhala mmudzi wa Biyala kwa mfumu yayikulu N
gabu ku Chikwawa apephedwa kuonetsa chikondi komanso kukhala bwino ndi anzawo mu nyengo ino yomwe a khirisitu amakumbukira infa komanso kuuka kwa Ambuye Yesu Khirisitu.
Mkulu wa sukulu ya nkombaphala ya Chisa, a Michael Ndelemani ndi omwe anayakhula izi pomwe sukuluyi mogwirizana ndi anthu ena imasangalala nyengo ya kuuka kwa ambuye Yesu khirisitu mmudzi mwa Biyala m
bomali.
Iwo anati ndikofunika kuti anthu alingalire za chikondi chomwe Yesu anationetsera ndipo akhale achikondi kwa anzawo pofunirana mafuno abwino. Powonjezera apo a Ndelemani anati sukulu ya Chisa inachiona cha nzeru kuti pomwe ikupereka maphunziro a nkombaphala kwa ana ang`ono angawanenso mawu opatsa moyo ndi makolo omwe amalera anawa.
Poyakhulapo a Enock Biyala omwe ndi mfumu ya mudziwu anati ndi osangalala ndi zomwe sukulu ya Chisa yapanga ponena kuti izi zapangitsa anthu ochuluka kubwera pamodzi kudzanva mawu a chauta zomwe zipangitse kuti pakhale kudalirana pamene akugwira tchito zosiyasiyana za chitukuko.
Mwazina ku mwambowu kunali ubatizo, kudyera pamodzi, kugawana mawu a Mulungu, Kuvina, masewero a mpira komanso kuonera kanena wa masautso a Yesu Khirisitu.
Kupatula kupereka maphunziro kwa ana a nkombaphala, sukulu ya Chisa imaphunzitsanso amayi maluso osiyanasiyana kuti akhale odzidalira komanso kugwira ntchito ndi achinyamata madera a kumidzi.
Sukulu ya mkombaphala ya ulere ya Chisa inatsekulidwa m`chaka cha 2018 pofuna kuchepetsa mavuto omwe ana okhala madera akumidzi amakumana nawo. Sukuluyi ikupezeka maboma a Chiradzulu, Balaka komanso Chikwawa.