Sat. Apr 20th, 2024

Kukanirana Kwabuka Pa Ndalama Zomwe Zinaonongedwa Ku UNGA

By Suleman Chitera Nov4,2022

Akuluakulu m’boma akukanirana komanso kukankhirana zokhudza lipoti la ndalama zomwe zidagwira ntchito ku mkumano wa United Nations General Assembly m’dziko la America komwe President Lazarus Chakwera ndi anthu ena 37 adapita.

Pafupifupi mwezi watha tsopano President Chakwera atabwera ku ulendowu koma nduna zake zikuchita jenkha kupereka lipoti za momwe misonkho ya aMalawi idagwilira ntchito.

Poyambilira, nduna zinayi motsogozedwa ndi m’neneri wa boma, Gospel Kazako zidalephera kuyankha mafunso a olemba nkhani ndipo zidati nduna yaza chuma, Sosten Gwengwe ndi yomwe ipereke lipoti-li.

Koma masiku angapo apitawa, akuluakulu ku unduna waza chuma adati iwo ntchito yawo nkupereka ndalama ku maunduna basi osati malipoti pa momwe ndalama-zi zagwilira ntchito.

Izi zikuchitika pomwe malipoti akuti ma allowance a anthu omwe adapita ku ulendowu adawakweza ndi 50 percent.

Koma mkulu wa bungwe la Centre for Social Accountability and Transparency-CSAT, Willy Kambwandira adati nzomvetsa chisoni kuti adindo akubisa zinthu zomwe ndizokhudza aMalawi zomwe anati zikusemphana ndi mfundo za boma zochita zinthu poyera.

Boma lidalepheranso kupereka lipoti lokhudza ndalama zomwe zidagwira ntchito pa mwambo wa chaka chino okondwera kuti dziko lino latha zaka 58 lili pa ufulu odzilamulira lokha.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

President Lazarus Chakwera has officially opened the Blantyre International Cancer Centre, The private health facility, has been constructed by the Thomson and Barbara Mpinganjira Foundation