Read Time:24 Second
Bwalo la magistrate ku Blantyre latulutsa pa belo yemwe anali wachiwiri kwa komishonala wa bungwe lotolela msonkho la MRA a Roza Mbilizi ndi anzawo ena awiri
Anthuwa anawamanga kaamba kowaganizira kuti adagwiritsa ntchito molakwika nambala yopelekera msonkho (TPIN) ya mtsogoleli wakale wa dziko lino a Peter Mutharika.
Bwaloli lalamula atatuwa kuti alipile K 350,000 ngati chikole komanso kuti apeleke ku bwaloli zikalata zawo zoyendera komanso anthuwa auzidwa kuti azikaonekera ku mafesi a ACB pa sabata ziwiri zili zonse
![](https://malawifreedomnetwork.com/wp-content/litespeed/avatar/ef805a2786e811efab4fadb5f19ba0ba.jpg?ver=1722052409)