Wed. May 1st, 2024

Mbiri Ya Moyo Wa Joseph Nkasa

Jimmy Joseph Kalekeni Nkasa anabadwa pa 3 DisembaIa mu 1967 m’boma la Zomba. Iye anabadwira m’dera lotchedwa Moleni ndipo ndi wachitatu kubadwa m’banja la ana anayi (amuna awiri ndi akazi awiri).

Katswiriyu anabadwira m’banja losauka zedi ndipo ali wachichepere amagwira maganyu n’cholinga choti azipeza zinthu zina m’moyo. Bambo ake anali woluka malichero ndi mabasiketi. Bambowa anaphunzitsa mwana waoyu lusoli ndipo anali kuthandizana kuti banja lizipeza chakudya.

M’zaka za m’ma 1970, makoIo ake anapeza maIo m’boma Ia Machinga. Banjali linakhazikika kwa mfumu yaikulu Sitola. Izi zinachititsa kuti boma la Machinga lisandukenso kwao.

Chifukwa chosowa chithandizo cha chuma, Joseph sanapite patali ndi sukulu. Iye anaisiya ali sitandade 8.

Nkasa anayamba kuyimba ali wachichepere mu ‘choir’ ya mpingo omwe ankapemphera otchedwa Full Gospel Church of God. M’chaka cha 1999 kunali msonkhano wapachaka wampingowu ndipo ‘choir’ yake linayimba modabwitsa kuposa ena. Izi zinachititsa kuti Nkasa apeze mwayi ndikuthandizidwa. Anthu omwe anali pamwamboyu anasonkha ndalama ndi zovala n’kumupatsa. Kenako, anajambula chimbale chake choyamba chauzimu pogwiritsa ntchito ndaIama yomwe anthu achifundowo anamupatsa.

Asanatulutse chimbale cha Wayenda Wapenga, Phungu anali atatulutsa kale zimbale pafupifupi zisanu. Zina mwa izo ndi Ndigwireni Dzanja, Kutha Kwafika, Messiah ndi Kupupuluma. Kuchokera pa chimbale cha Wayenda Wapenga, Nkasa watulutsa zimbale zina zoposa zinayi ndipo zina ndi monga Mizimu, Mamillionaire ndi Tigwirane Manja.

Katswiriyu amatchuka ndi dzina loti phungu chifukwa cha malangizo omwe amapezeka m’nyimbo zake.

Nkasa ali pabanja ndipo anadaIitsidwa ndi anayi asanu ndi atatu.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window