Sun. Apr 28th, 2024

Olowa Kumene Adikire Zaka Ziwiri–MCP

MUNTHU AMENE WANGOLOWA KUMENE MU CHIPANI CHA MCP ALIBE MWAYI OZAPIKISANA PA ZISANKHO MU KOMITI YAIKULU CHAKA CHINO

Chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chamanga mfundo yoti yemwe akufuna mpando mu komiti yaikulu ya chipanichi adzikhala kuti anakhalapo pa udindo mchipanichi kwa zaka ziwiri.

Anthu ena omwe atitsina khutu, ati komiti yaikulu ya chipanichi ndi yomwe yagwirizana izi pa msokhano wake omwe inachititsa lero mu mnzinda wa Lilongwe.

Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera, yemwenso ndi pulezidenti wa chipanichi, anali nawo pa zokambilanazo.

Otitsina khutuwo, omwe anali nawo pa nkumanowo koma anapempha kuti tisawatchule, ati mmodzi mwa nthumwi anabweretsa mfundoyi kugulu ndipo ena anaiikila kumbuyo, kenako komitiyo nkuivomereza.

Iwo anati zaka ziwirizo zikhale zoti munthu anakhalapo pa mpando uli onse omwe unakhazikitsidwa mu malamulo aakulu a chipanichi.

Izi zikutanthauza kuti anthu ongolowa kumene mchipanichi alibe mwayi opikisana nawo pa zisankho za komiti yaikulu zomwe zichitike chaka chino.

Pakali pano mneneri wa MCP a Ezekiel Ching’oma akana kuikapo mlomo pa nkhaniyi.

Iwo ati chipanichi chitulutsa kalata yofotokoza tsatanetsatane wa zomwe akambiranazo.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi business tycoon Simbi Phiri disassociates himself from forming up “Congress for Democrats”

Business Mogul Simbi Ashan Phiri who is Executive Chairman of Katho Civils has disassociated himself from social media rumours that Read more

The British NCA Operations In Malawi Remain Questionable, Britons Aim To Topple Tonse Government

Exposed! British NCA bankrolls PIJ to victimize successful business persons, politicians, judges in Malawi The truth be told! The establishment Read more

Mirece supports land reclamation bought by foreigners

Reverend Flywell Somanje…. this is the way to go A governance and human rights organization, the Millennium Information and Resource Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open