Chipani chatsopano cha People’s Development Party – PDP chatsegula khomo kwa omwe akufuna kudzachiyimila ngati aphungu komanso ma-khansala.
M’chikalata chomwe wasindikiza n’neneri wa wachipanichi Rhodes Msonkho PDP yati yachita izi kuti omwe akufuna kudzayimila maudindowa ayifikile.
PDP ndi chipani chomwe angochilembetsa kumene ndipo yemwe akuchitsogelera ndi Kondwani Nankhumwa.
Pamenepa Msonkho wati omwe ali ndi chidwi m’maudindowa afikile PDP kukalembetsa m’kaundula