FB IMG 1660799059295

“Penapake Pakayenda Bwino Zambia Tidya Nayo Bwino”-Dr Chakwera.

President Lazarus Chakwera dzulo lachitatu anapanga mkumano wapadera ndi President wa dziko la Zambia Hakainde Hichilema pambali pa mkumano wa atsogoleri amu bungwe la SADC omwe uli mkati m’dziko la Democratic Republic of Congo.

Polemba pa tsamba lawo la Facebook, Dr Chakwera anati iwo ndi a Hichilema anakambilana nkhani zingapo kuphatikizapo ndondomeko yolimbikitsa ntchito za malonda pakati pa maiko awiliwa.

Kumbali yake, Dr Chakwera anayamikira a Hichilema komanso dziko la Zambia pazomwe lidachita ponjata mzika ya dziko la China yotchedwa Lu Ke (Susu) yomwe pakadali pano ili kuno kumudzi kuyankha milandu yopanga za kusayeluzika pogwilitsa ntchito ana akwa Njewa Ku Lilongwe.

Iwo anayamikilanso boma la Zambia kaamba kothandizapo pa ndondomeko yotumiza kuno kumudzi matupi a ogwira ntchito atatu a bungwe la Central Medical stores trust omwe adafa pangozi ya galimoto ku Zambia.

More From Author

FB IMG 1660766385110 300x225

3 ARRESTED OVER WITCHCRAFT ACCUSATIONS IN DOWA

FB IMG 1660814166642 300x201

Mombera University Construction Ready To Start

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ella Brown

Project Manager

Darkness cannot drive out darkness; only light can do that. Hate cannot drive out hate: only love can do that.