Mchithunzi, Kantukule kulandira President Chakwera pa Kamuzu International Airport}.
Gulu lomwe likudzitchula kuti General Membership of Malawi Congress Party laonetsa kudabwa kuti President Lazarus Chakwera adasankha nduna yaza ntchito Vera Kantukule kuyang’anira dziko pomwe ankapita ku Mozambique m’mwezi wa April chaka chino chikhalirecho ndunayi siya MCP komanso ilibe udindo ulionse mchipanichi.
Iwo akuti a Chakwera akanatha kusankha amai ena mchipanichi omwenso ali nkuthekera pomwe ati pa ndale mtsogoleriyu adaphonya.
Izi ndi malinga ndi kalata yomwe gululi latulutsa pomwe latinso anthu ochulula omwe analembedwa ntchito ku nyumba ya boma {State House} ndi a mpingo wa Assemblies of God.
Kalatayi yomwe yasainidwa ndi m’neneri wake, Zinenani Magola komanso wapampando, Alex Major yatinso mamembalawa ndiokhudzidwa ndi zomwe adanena m’neneri wa MCP, Maurice Munthali kuti mtsonkhano waukulu wa chipanichi udzachitika mu 2024 osati 2023 zomwe akuti nzosemphana ndi malamulo awo.
Read also: DPP opts for coalition path ahead of September 16 Elections
Read also: Kalindo says Chakwera is the worst leader in Malawi
Read also: “Yakwiya Ndi Mizimu!”: Nelson Kuchima and Associates Face Community Justice
“Tikupemphanso Chakwera kuti azikwanilitsa zomwe amayankhula komanso kumvera zomwe amalangizidwa,” yatero kalatayi.
M’neneri wa chipani cha MCP komanso wa President Chakwera, Anthony Kasunda sadayankhulepo pa kalatayi.
{
Read also: Iran Launches Ballistic Missiles at U.S. Base in Saudi Arabia in Direct Retaliation
Read also: Unima Student Sentenced 22 Months Imprisonment For Theft





