1002190420

Phungu wa dera la Machinga East a Esther Jolobala wati mngodabwa kuti nthambi ya NRB siidayambebe kulemekeza chigamulo cha khothi chomwe chinapelekedwa Lachisanu lapitalo.

Mwa zina, khothi lidalamula NRB kumalembetsa anthu ziphaso zaunzika mmalo momwe bungwe loyendetsa chisankho la MEC likuchitira kalembera wa chisankho.

A Jolobala ati: “NRB siinatsegule centre ina iliyonse ku Machinga kuti anthu azikalembetsapo. Kodi kumeneko ndi kutsatira chigamulo cha khothi? Kodi atsegula liti popeza nthawi yomwe adzitsegula ikhala kuti gawo loyamba la kalembera yatha?”

Gawo loyamba la kalembera wa voti likuyembekezeka kutha pa 3 November chaka chino.

Koma NRB yati itsegula malo olembetsera kaundula wa nzika owonjezera ngati njira imodzi yotsatira chigamulo cha bwalo lalikulu.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  Smartmatic: Controversy, legal battles, and the future of election technology

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *