Malawi Freedom Network
Giving you daily news that rock the world

Malawi Ikumana Ndi Senegal

FeaturedInternationalSports

Timu ya masewero a mpira wa miyendo ya dziko lino usiku wa lero ili ndi masewero a mtima bii pomwe ikhale ikukumana ndi timu ya Senegal.

Awa ndi masewero odzigulira malo ku mpikisano wa Afcon wa chaka cha mawa omwe ukachitikire m’dziko la Morocco.

Timu ya Malawi ikuyenera mwa njira iliyonse kupambana masewerowo kuti loto lake lokafika ku Morocco likhalepobe.

Pa masewero awiri omwe timuyi yasewera mu ndimeyi, Flames yagonja masewero onse.

Mphunzitsi wa timuyi Patrick Mabedi wati timu yakeyi itha kupambana masewerowa pokhapokha osewera ataikirapo mtima.

Matimuwa akakumana lero ku Senegal, akuyembekezeka kubwerezana lachiwiri likubwerali pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.

M’masewero a mu gulu lomweli, usiku wapitawu Burkina Faso yababada Burundi 4-1.

Related posts

Parliament’s Legal Affairs Committee Launches Inquiry into Allegations Against High Court Judge Ken Manda

By Burnett Munthali

Kajawa’s Midas Touch: Bangwe All Stars Rises from the Ashes

Malawi Freedom Network

DPP’s Ben Phiri Raises Concerns Over Government’s Inaction on Chilima Plane Crash Investigation

By Suleman Chitera

After rejection in SA, Chidimma Adetshina wins Miss Universe Nigeria

Malawi Freedom Network

North Journalists Celebrate Mother’s Day with Hospital Visit 

Malawi Freedom Network

Tanzanian President Suluhu To Visit Malawi

Malawi Freedom Network

Leave a Comment

Leave a review

This website uses cookies to improve your experience. We'll assume you're ok with this, but you can opt-out if you wish. Accept Read More