FB IMG 1728623249589

Timu ya masewero a mpira wa miyendo ya dziko lino usiku wa lero ili ndi masewero a mtima bii pomwe ikhale ikukumana ndi timu ya Senegal.

Awa ndi masewero odzigulira malo ku mpikisano wa Afcon wa chaka cha mawa omwe ukachitikire m’dziko la Morocco.

Timu ya Malawi ikuyenera mwa njira iliyonse kupambana masewerowo kuti loto lake lokafika ku Morocco likhalepobe.

Pa masewero awiri omwe timuyi yasewera mu ndimeyi, Flames yagonja masewero onse.

Mphunzitsi wa timuyi Patrick Mabedi wati timu yakeyi itha kupambana masewerowa pokhapokha osewera ataikirapo mtima.

Matimuwa akakumana lero ku Senegal, akuyembekezeka kubwerezana lachiwiri likubwerali pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.

M’masewero a mu gulu lomweli, usiku wapitawu Burkina Faso yababada Burundi 4-1.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  Malawi rolls out dual citizenship to Malawians living in Zimbabwe

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *