Thu. Apr 25th, 2024

APOLISI AMANGA NURSE KAMBA KONYOZA CHAKWERA PA WHATSAPP

By Suleman Chitera May2,2022

A Malawi Police amanga nurse wa chipatala cha Ntcheu District Hospital, a Chidawawa Mainje, a dzaka zakubadwa 39 powaganizira kuti ananyoza mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera kudzera pa tsamba la mchezo la Whatsapp.
News update
Yapeza kuti a Mainje amachita mtsuso (debate) ndi anzawo pa whatsapp group. Mtsusowo unali wa ndale, okamba za momwe zinthu zikuyendera m’dziko muno mu ulamuliro wa Lazarus Chakwera ndi wachiwiri wake, Saulos Chilima.

Mtsusowo unakolera moto, ndipo Mainje anatemetsa nkhwangwa pa mwala kuti zinthu siziri bwino m’dziko muno, ndipo Chakwera walephera kuyendetsa dziko lino ngati mtsogoleri.

Ali mkati mwa mtsusowo, munthu wina pa group-yo anajambura (screenshot) zomwe anayankhura Mainje, ndipo adadziwitsa mkulu wina wa boma la Chakwera.

Mkuluyo atawona ma screenshot-wo anakwiya kwambiri, ndipo posakhalitsa galimoto ya police inabwera kuchokera komwe ku likulu la police ku area 30 mu mzinda wa Lilongwe, ndipo linamanga Mainje.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open