APOLISI AMANGA NURSE KAMBA KONYOZA CHAKWERA PA WHATSAPP

A Malawi Police amanga nurse wa chipatala cha Ntcheu District Hospital, a Chidawawa Mainje, a dzaka zakubadwa 39 powaganizira kuti ananyoza mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera kudzera pa tsamba la mchezo la Whatsapp.
News update
Yapeza kuti a Mainje amachita mtsuso (debate) ndi anzawo pa whatsapp group. Mtsusowo unali wa ndale, okamba za momwe zinthu zikuyendera m’dziko muno mu ulamuliro wa Lazarus Chakwera ndi wachiwiri wake, Saulos Chilima.

Mtsusowo unakolera moto, ndipo Mainje anatemetsa nkhwangwa pa mwala kuti zinthu siziri bwino m’dziko muno, ndipo Chakwera walephera kuyendetsa dziko lino ngati mtsogoleri.

Ali mkati mwa mtsusowo, munthu wina pa group-yo anajambura (screenshot) zomwe anayankhura Mainje, ndipo adadziwitsa mkulu wina wa boma la Chakwera.

Mkuluyo atawona ma screenshot-wo anakwiya kwambiri, ndipo posakhalitsa galimoto ya police inabwera kuchokera komwe ku likulu la police ku area 30 mu mzinda wa Lilongwe, ndipo linamanga Mainje.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *