Thu. Apr 25th, 2024

Buluma Wasiya Ntchito Ndipo Wayamba Kuulula Zobisika

By Suleman Chitera Nov17,2022

Yemwe amagwirizira ngati mkulu wa bungwe la NOCMA, Hellen Buluma watula pansi udindo-wu koma waulula zina zobisika zomwe akuti akuluakulu ena m’boma komanso andale akhala akumukakamiza kuchita ngakhale nzosemphana ndi malamulo.

Izi zili mukalata yopuma pa ntchito yomwe a Buluma alembera wapampando wa board ya bungweli, Colleen Zamba, yemwenso ndi mlembi mu ofesi ya mtsogoleri wa dziko ndi nduna zake.

ABuluma ati a Zamba komanso mlembi ku unduna waza mphamvu, Alfonso Chikuni komanso andale ena akhala akuwapanikiza komanso kuwaopseza kuti apereke ma contract mwa chinyengo ku kampani za ku mtima kwa adindowa.

Mu kalata yomwe taona, a Buluma atinso akhala akuwakakamiza kuti apereke malo a Chipoka ku Salima kwa mkulu wina wa ndale m’chipani cha MCP kuti adzichita malonda koma mwautambwali ndi ochita malonda ena akunja.

“Mtsogoleri wadziko lino wakhala akulankhula motsutsana ndi m’chitidwe-wu ndipo adandilangiza kuti ndidzichita zinthu nthawi zonse molingana ndi malamulo pogwira ntchito. Koma inu madam mwakhala mukundipanikiza ndi zosiyana ndi zomwe a pulezidenti amanena maka pa nkhani yolowelera pa ntchito,” yatero kalatayi.

Mai Zamba atsimikiza za kusiya ntchito kwa a Buluma koma sadafotokoze zambiri pomwe a Buluma sayankhe pomwe timafuna kumva zambiri kuchokera kea iwo pa nkhani-yi.

Izi zadza pomwe board ya NOCMA yakhala ikunyozera kumvera zomwe ofesi ya Ombudsman idanena kuti ichotse ntchito mai Buluma ati kamba koti panalibe kutsatira ndondomeko komanso malamulo pa nthawi yomwe ankawalemba ntchito.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open