Mtsogoleri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG) Prophet Shepherd Bushiri wapereka chimanga kwa maanja oposera 1200 omwe akuvutika ndi njala m’boma la Mangochi.
A Bushiri ati akudziwa kuti anthu ambiri akufunika thandizo la chimanga m’madera ambiri m’dziko muno ndipo ati ichi nchifukwa chake akupitilira ndi ntchito yogawa chimangachi.
Iwo ati ntchitoyi ifikira maboma onse a dziko lino ndipo apempha anthu ena onse akuchita ntchito ya mtunduwu kuti apitirize pofuna kufikira a Malawi ochuluka omwe akuvutika ndi njala.
“Galimoto za mtundu wa truck zopitirira khumi zili kale m’maboma a Dowa, Rumphi, Nkhotakota ndi ena komwenso tikhale tikufikira anthu ndi thandizo la chimanga, choncho ndipemphe anzanga ena omwe akupanga ntchito yofanana ndi yomwe tikugwira kuti tigwirane manja pofuna kuombola Malawi,” atero a Bushiri.
Mmodzi mwa anthu omwe alandira nawo thandizoli a Dorcas Baluti a mdera la mfumu yaikulu Namkumba ayamikira a Bushiri kamba kathandizoli ponena kuti liwapulumutsa ku njala yomwe ikuwasautsa kamba koti chimanga chomwe adalima m’minda yawo chidauma kamba ka ng’amba yomwe inali m’dziko muno.