Sun. May 5th, 2024

Chakwera Aonetse Kuti Siwolephera Kutumikira A Malawi

Mabungwe omwe si aboma ku Kasungu ati nthawi yakwana tsopano kuti mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera aonetse kuti siwolephera kutumikira a Malawi.

Wapampando wa mabungwewa a Braxton Banda wati a Chakwera akuyenera kuchotsa ntchito mkulu wa nthambi ya immigration a Charles Kalumbo pa chimpwirikiti chokhudza ma passport.

A Banda akukhulupilira kuti izi zithandizira kuti anthu asataye chikhulupiliro mwa utsogoleri wa a Chakwera maka pomwe chisankho cha chaka cha mawa chayamba kale kununkhira.

“Kulephera kulondoloza ndikupezanso mayankho a vuto lomwe lili ku nthambi ya immigration, anthu ena akuloza chala mtsogoleri wa dziko linoyu.

“Ichi ndi chifukwa chake ife a mabungwe tikuwapempha komanso kuwatsina khutu a pulezidenti kuti achotse ntchito mkuluyu, pofuna kuteteza mbiri yawo komanso kukonza zinthu,” atero a Banda.

Pempholi ladza pomwe gulu lina la mzika zokhudziwa zakonza m’bindikiro ku ofesi za immigration pa 12 March pofuna kukamiza a Chakwera kuti achotse ntchito a Kalumo komanso nduna ya chitetezo a Ken Zikhale Ng’oma pa nkhani yomweyi.

Koma akuluakulu ku nthambi ya immigration ati akuyesetsa kuti athane ndi vutoli asanathe masiku 21 omwe a Chakwera adawapatsa kuti akonze zinthu..

Related Posts
David Bisnowaty Israeli-Born Malawi Parliament Member: Actions, Not Words, Will Change Africa for the Better

Malawi MP David Bisnowaty. How does the Israeli-born son of an eastern European Holocaust survivor end up as a parliament Read more

David Bisnowaty former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country

Political cum and former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country https://youtu.be/S20UYlVcHs8

AGHF Feeds Patients, Guardians At Mangochi District Hospital

A giving hand foundation is a local organisation working in various programs in Malawi. On Thursday the organization together with Read more

NBM Donates K100 Million Towards Forest Restoration

National Bank of Malawi has committed K100 million for preservation and restoration of 6 natural resources in the country by Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window