Wolemba: Noel Mkwaila, BLANTYRE
President Lazarus Chakwera wayamikira mkulu ochita malonda a Thom Mpinganjira pokhazikitsa chipatala chapamwamba chothana ndi nthenda ya cancer munzinda wa Blantyre chotchedwa International Blantyre Cancer Centre-IBCC.
A Chakwera ati izi zithandizira kwambiri ku nkhondo yolimbana ndi nthendayi pomwe aMalawi ena osauka amangodzifera popeza sangakwanitse kupita m’maiko ena monga India kukapeza thandizo.
Iwo ati akukhulupilira kuti dziko lino lidzakhala litayamba kuthandiza anthu odwala cancer mwalokha pofika 2030.
A Mpinganjira ati malingaliro omanga chipatalachi anawadzera, mkazi wawo atamwalira ku nthenda ya cancer zaka zisanu zapitazo ndipo akuzindikira bwino za zokhoma zomwe zilipo kaamba kakusowa kwa chipatalachi mdziko muno.
“Ndili ndi chimwemwe kwambiri kuti chipatalachi chatheka ndipo ndithokoze boma kaamba ka thandizo lomwe limapereka pa nthawi yomanga chipatalachi,” atero a Mpinganjira.
Chipatalachi chamangidwa ndi bungwe la Thomson and Barbra Foundation komanso abwenzi ena.
Pakadalipano, ndalama zoposa K9 billion ndi zomwe zagwira ntchito pa chipatalachi.