Katswiri pa nkhani za ndale ndi ulamuliro wabwino mdziko muno a Dr George Chaima alangiza wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino a Dr Saulos Chilima kuti ayambe kukonzekela zodzayima pa chisankho cha chaka cha mawa ngati mtsogoleri wa chipani cha UTM posatengera za mgwirizano omwe ulipo pakatipa iwo ndi Dr. Lazarus Chakwera.
A Chaima ati a Chilima achedwa akadalira kwambiri mgwirizano wawo omwe anagwirizana pa zisankho za chaka cha 2020.
Malingana ndi a Chaima ati zomwe chapanga chipani cha Malawi Congress, kunena kuti Dr. Chakwera adzayimira ngati mtsogoleri wachipanichi chaka cha mawa sikulakwa kuli konse.