Thu. Apr 25th, 2024

MCP General Membership Idabwa Ndi Ulamuliro Wa Chakwera

By Suleman Chitera Jun2,2022

Mchithunzi, Kantukule kulandira President Chakwera pa Kamuzu International Airport}.

Gulu lomwe likudzitchula kuti General Membership of Malawi Congress Party laonetsa kudabwa kuti President Lazarus Chakwera adasankha nduna yaza ntchito Vera Kantukule kuyang’anira dziko pomwe ankapita ku Mozambique m’mwezi wa April chaka chino chikhalirecho ndunayi siya MCP komanso ilibe udindo ulionse mchipanichi.

Iwo akuti a Chakwera akanatha kusankha amai ena mchipanichi omwenso ali nkuthekera pomwe ati pa ndale mtsogoleriyu adaphonya.

Izi ndi malinga ndi kalata yomwe gululi latulutsa pomwe latinso anthu ochulula omwe analembedwa ntchito ku nyumba ya boma {State House} ndi a mpingo wa Assemblies of God.

Kalatayi yomwe yasainidwa ndi m’neneri wake, Zinenani Magola komanso wapampando, Alex Major yatinso mamembalawa ndiokhudzidwa ndi zomwe adanena m’neneri wa MCP, Maurice Munthali kuti mtsonkhano waukulu wa chipanichi udzachitika mu 2024 osati 2023 zomwe akuti nzosemphana ndi malamulo awo.

“Tikupemphanso Chakwera kuti azikwanilitsa zomwe amayankhula komanso kumvera zomwe amalangizidwa,” yatero kalatayi.

M’neneri wa chipani cha MCP komanso wa President Chakwera, Anthony Kasunda sadayankhulepo pa kalatayi.

{

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open