Fri. May 3rd, 2024

Mutharika Achezera Asilamu Pa Mzikiti Mangochi

PRESIDENT MUTHARIKA ACHEZERA ASILAMU A PA MZIKITI WA MANGOCHI MAIN MOSQUE

Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemwenso ndi Mtsogoleri wa Chipani cha Democratic Progressive Party-DPP, His Excellency Professor Arthur Peter Mutharika, lero chakusanaku anakachezera asilamu pa Mzikiti wa Mangochi Main Mosque ntown ya Mangochi.

Mwachizowezi, a Mutharika anachezera komanso kuwalimbikisa abale ndi alongo achisilamu amene padakali pano ali mu nyenyo Ramadan. Iwo ananena kuti nyenyo ya Ramadan ndi yofunikira kwambiri imene ili nthawi imene otsatira chipembezo Cha chisilamu amayandikana ndi Allah posala kudya, komanso kuchita ntchito zachifundo (Zakaati).

Pofuna kuwonetsa chikondi chawo, A Mutharika agawa zakudya monga mpunga, sugar komanso ufa zoti anthu pa mzikitipa azigwiritsa ntchito amakamasula Ramadan.

Paulendowu, Iwo anaperekezedwa ndi Olemekezeka Sameer Suleman MP, olemekezeka a Ralph Jooma, Sheik Salire Saidi komanso akulu akulu ampingo wa chisilamu m’bomali.

Poyankhulapo, mmodzi mwa akuluakulu a chipembedzo cha chisilamu womwe anali nawo pa mwambowu anati Professor Mutharika wakhala akuchita izi chaka ndi chaka ndipo asilamu wonse ku Mangochi ndiwokondwa chifukwa akawona Professor Mutharika akuwayendera amalimbikitsika ngakhale akudutsa mmavuto osiyanasiyana.

A Mutharika womwe ali ndi achibale ambiri omwe Ali achipembedzo cha chisilamu afunira asilamu wonse mdziko muno pamene ali munyengo imeneyi ya Ramadani

Related Posts

David Bisnowaty Israeli-Born Malawi Parliament Member: Actions, Not Words, Will Change Africa for the Better

Malawi MP David Bisnowaty. How does the Israeli-born son of an eastern European Holocaust survivor end up as a parliament Read more

David Bisnowaty former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country

Political cum and former Member Of Parliament for Lilongwe City Centre break silence on political situation in the country https://youtu.be/S20UYlVcHs8

AGHF Feeds Patients, Guardians At Mangochi District Hospital

A giving hand foundation is a local organisation working in various programs in Malawi. On Thursday the organization together with Read more

Mirece supports land reclamation bought by foreigners

Reverend Flywell Somanje…. this is the way to go A governance and human rights organization, the Millennium Information and Resource Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window