Malawi Freedom Network

ONYAMULA MAKALA AMUNJATA KU SALIMA

Apolisi ku Salima amanga bambo wa zaka 30, Yotamu Mapulanga pomuganizira kuti amazembetsa makala ndipo amulandanso galimoto yomwe ananyamulira makalawo ponena kuti inalibe kalata zoyenera.

M’neneri wa apolisi m’bomalo, Sub-Inspector Jacob Khembo wati apolisi alanda galimoto ya 15 ton ya mtundu wa Scania yomwe nambala yake ndi KK 7020, yomwe inali yodzadza ndi matumba a makala.

Sub-Inspector Khembo wati apolisi anagwira mkukuyu anthu ena atawatsina khutu koma pano ntchito yofufuza ili mkati kuti agwire anthu ena omwe athawa.

Mapulanga amachokera m’mudzi wa Chilipa, mfumu yaikulu Chimwala, m’boma la Mangochi.

Iye akawonekera ku bwalo zofufuza za apolisi zikatha.

Leave a Comment

* By using this form you agree with the storage and handling of your data by this website.

Leave a review

Malawi Freedom Network
Giving you daily news that rock the world

This website uses cookies to improve your experience. We'll assume you're ok with this, but you can opt-out if you wish. Accept Read More