Thu. Apr 25th, 2024

Phungu Wa Nyumba Ya Malamulo Wamangidwa Atagunda Wa Traffic

By Suleman Chitera Oct25,2022

Apolisi amanga phungu wa nyumba ya malamulo wa dera lakumpoto chakummawa kwa boma la Ntcheu, Arthur Chipungu pomuganizira kuti adagunda ndikuvulaza wa polisi wa pansewu yemwe akuti adalephera kumupatsa thandizo loyenera.

M’neneri wa polisi, Peter Kalaya wati mkuluyu wakhala akuthawathawa kwa masiku asanu ndi limodzi chichitikireni nkhani-yi Lachiwiri sabata yatha.

Kalaya wati amanga phungu-yu atadzipereka ekha ku likulu la polisi munzinda wa Lilongwe, komwe anabwera ndi loya wake.

Chipungu akumuganizira kuti adachita za chipongwezi pa malo a pakati pa bwalo la zamasewero la Bingu ndi Area 18 Interchange munzindawu.

Pakadalipano, Kalaya wati apolisi akusunga mkuluyu ku polisi ya Lingadzi ndipo akaonekera kubwalo la milandu mawa, Lachiwiri.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open