STATE HOUSE ILENGEZA IMFA YA MIRIAM CHAKWERA

“`President Lazarus Chakwera wataya mlongo wawo Mirriam Chakwera yemwe wamwalira lero.

Mlembi wa atolankhani a President Anthony Kasunda walengeza za imfa ya mlongo wake wa Chakwera mwachidule.

A Kasunda adaonjeza kuti Chakwera wathetsa nthawi yomweyo zokambirana zake ndi anthu.
“Mtsogoleri wa dziko lino ayambiranso zokambirana zake ndi anthu akayika maliro a mlongo wawo, zomwe zikuyenera kuchitika pa Epulo 20 m’mudzi mwa Manase ku Mdika m’boma la Dowa,” adatero Kasunda.“`

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *