IMG 20220514 WA0089

Nduna yowona zokopa alendo yomwenso ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha UTM, Michael Usi awuza President Lazarus chakwera kuti chipani cha UTM chilibe lingaliro lotuluka mu mgwilizano wa Tonse alliance ngakhale pali kagulu kena komwe kakufuna zinthu zitero.

A Usi ati kukakamiza chipani cha UTM kutuluka mu mgwilizano wa Tonse mchimodzimodzi kukakamiza munthu kuti atsike mu bwato lili pakati pa nyanja.

A Usi alumbila ponena kuti UTM ipitiliza kulemekeza mgwilizano wa Tonse.

Iwo ayankhula izi pa mwambo okumbukira mtsogoleri oyamba wa dziko lino Dr Hastings Kamuzu Banda Ku Lilongwe.

Poyankhulapo, ndunayi inauzanso Dr chakwera kuti achotse ntchito kagulu kena ka anthu komwe kakufuna kusokoneza boma lake.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *