Technical sub committee ya FAM yati mphunzitsi watimu ya FCB Nyasa Bullets Kalisto Pasuwa ndiye ali oyenera kukhala mphunzitsi watimu ya Flames mongogwilizila.

Izi zakambidwa dzulo ku Mpira Village ku Chiwembe munzinda wa Blantyre pomwe komitiyi imaunikira tsogolo la timu ya mpira wamiyendo ya dziko lino.

Matsiku apitawa bungwe la FAM linalengeza kuti agwilizana ndi mphunzitsi watimu ya Flames Mario Marian Marinica kuti saonjezelaso contract pomwe contract yake ikutha kumathero kwa mwezi uno.

Anthu okonda masewero mdziko muno akhala akuonesa kusakondwa ndi kaseweledwe ka timu ya Flames pansi pa Mario Marinica.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *