Asilikali alephera kupherera chipolopolo cha Mapale

Nkhope za ochemelera a FCB Nyasa Big Bullets zikupitilirabe kulemedwa ndichisangalaro pamene timuyi yagonjetsa Moyale Barracks 3-1 mumasemifainolo a FDH Bank Cup pa bwalo la Bingu mu nzinda wa Lilongwe.

Chipambanochi chikudza, patangodutsa masiku atatu timu yovala zoyera ndi zofiirayi itagonjetsa Red Arrows ya m’dziko la Zambia 2-1 mumasewero oyamba a CAF Champions League.

Chigoli chimodzi kuchokera kwa Ephraim Kondowe komanso zigoli ziwiri kuchokera kwa Babatunde Adepoju, pamene Emmanuel Allan, ndi yemwe anagoletsa chigoli chopukutira misozi kwa asilikaliwa.

Potsatira chipambanochi, Mapale adzakumana ndi Blue Eagles FC mu ndime yotsiliza yampikisanowu.

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Please disable your adblocker or whitelist this site!