Nkhope za ochemelera a FCB Nyasa Big Bullets zikupitilirabe kulemedwa ndichisangalaro pamene timuyi yagonjetsa Moyale Barracks 3-1 mumasemifainolo a FDH Bank Cup pa bwalo la Bingu mu nzinda wa Lilongwe.

Chipambanochi chikudza, patangodutsa masiku atatu timu yovala zoyera ndi zofiirayi itagonjetsa Red Arrows ya m’dziko la Zambia 2-1 mumasewero oyamba a CAF Champions League.

Chigoli chimodzi kuchokera kwa Ephraim Kondowe komanso zigoli ziwiri kuchokera kwa Babatunde Adepoju, pamene Emmanuel Allan, ndi yemwe anagoletsa chigoli chopukutira misozi kwa asilikaliwa.

Potsatira chipambanochi, Mapale adzakumana ndi Blue Eagles FC mu ndime yotsiliza yampikisanowu.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *