Mphunzitsi wa timu ya FCB Nyasa Big Bullets wadandaula ndi kaimbilidwa komwe kadalipo masewero awo ndi timu ya Red Arrows loweruka lapitali.
Callisto Pasuwa wati ziganizo zina zomwe adachita oyimbira masewerowa ndi zomwe zidachititsa kuti timuyi igonje.
Pasuwa wapempha kuti chilungamo chidzikhalapo pa masewero ndi cholinga chakuti mpikisano udzikhala okomera matimu onse.
Elmabrouk Muhamad wa ku Libya ndi yemwe adaimbira masewero achibwereza omwe Bullets idagonja 2-0 pa bwalo la Heroes m’dziko la Zambia.
Kutsatira kugonjaku, Bullets idatuluka mpikisanowu 3-2 pa masewero awiri.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!