Mphunzitsi wa timu ya FCB Nyasa Big Bullets wadandaula ndi kaimbilidwa komwe kadalipo masewero awo ndi timu ya Red Arrows loweruka lapitali.

Callisto Pasuwa wati ziganizo zina zomwe adachita oyimbira masewerowa ndi zomwe zidachititsa kuti timuyi igonje.

Pasuwa wapempha kuti chilungamo chidzikhalapo pa masewero ndi cholinga chakuti mpikisano udzikhala okomera matimu onse.

Elmabrouk Muhamad wa ku Libya ndi yemwe adaimbira masewero achibwereza omwe Bullets idagonja 2-0 pa bwalo la Heroes m’dziko la Zambia.

Kutsatira kugonjaku, Bullets idatuluka mpikisanowu 3-2 pa masewero awiri.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *