FB IMG 1724987513142
FB IMG 1724987509522

Football Association of Malawi (FAM) yati khumbo lawo ndilofuna kutulutsa chiwerengero chochuluka cha aphunzitsi a mpira wamiyendo oti azitha kumpikisana ndi aphunzitsi omwe akuchita bwino kunja kwa dziko lino.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa FAM, Christopher Madalitso Kuyera, walankhula izi lero, lachinayi, pa 29 August 2024 ku Mpira Village ku Chiwembe mu nzinda wa Blantyre pomwe amatsegulira maphunziro a aphunzitsi omwe akufuna kupeza tsamba la CAF B.

Kuyera watinso maso mphenya abungweli ndiofuna kukhala ndi aphunzitsi aukadaulo pofuna kukwaniritsa lingaliro lawo losintha masewerowa.

Mkulu wa bungwe la aphunzitsi, Aubrey Nankhuni, wathokoza utsogoleri wa Fleetwood Haiya omwe wapanga kuthekera kokhala ndi maphunzirowa.

Nankhuni wati anali ndi mavuto potulutsa maina a anthu omwe akuchita maphunziro wa potengera kuti chiwerengero cha aphunzitsi omwe alibe tsamba la CAF B ndi chokwera.

M’modzi mwa anthu omwe amalankhula mmalo mwa aphunzitsiwa, Victor Mphande, wayamikira FAM komanso bungweli kamba kochititsa maphunzirowa.

Captain John Kaputa komanso Technical Director wa FAM, Benjamin Kumwenda ndi ena mwa aphunzitsi omwe akuchititsa maphunzirowa omwe ndi amasiku 90 mmalo mwa bungwe la CAF.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  TNM and SULOM complete disbursement of subventions today clubs

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *