FB IMG 1725626364772FB IMG 1725626364772

Mphunzitsi wa timu ya Malawi Patrick Mabedi wati ngati mphunzitsi pena zimayenera kuoneka ngati wamwano kuti zinthu zina ziyende.

Iye amayankhula izi poyankha mafunso kwa atolankhani pakutha pa masewero omwe timu ya Malawi yagonja 3-2 ndi Burundi.

Iye wati anthu ochemelera amaonera mpira mosiyana ndi momwe iwo ngati ophunzitsa amaonera.

Mabedi amayankha funso pa chifukwa chomwe amamutulutsira Yamikani Chester pomwe ochemelera amaona kuti akuthandiza timuyi.

Koma poyankhapo ngati alibe nkhawa ndi mkuwe omwe ochemelera amachita timuyi itagonja, iye adati sakutekeseka, akuti iwo akuwidwako ngati osewera ndipo mkuwe wa dzulo mwinaso unachepa.

Malawi ikuyembekezeka kusewera ndi Burkina Faso lachiwiri likubwerali m’dziko la Mali pa masewero ake a chiwiri mu ndime yodzigulira malo ku mpikisano wa 2025 Afcon.

Wolemba: Promise Thom

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  Mutharika showers Blantyre Synod pastors with cash and promises

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *