Malawi Freedom Network
Giving you daily news that rock the world

Malawi Ikumana Ndi Senegal

FeaturedInternationalSports

Timu ya masewero a mpira wa miyendo ya dziko lino usiku wa lero ili ndi masewero a mtima bii pomwe ikhale ikukumana ndi timu ya Senegal.

Awa ndi masewero odzigulira malo ku mpikisano wa Afcon wa chaka cha mawa omwe ukachitikire m’dziko la Morocco.

Timu ya Malawi ikuyenera mwa njira iliyonse kupambana masewerowo kuti loto lake lokafika ku Morocco likhalepobe.

Pa masewero awiri omwe timuyi yasewera mu ndimeyi, Flames yagonja masewero onse.

Mphunzitsi wa timuyi Patrick Mabedi wati timu yakeyi itha kupambana masewerowa pokhapokha osewera ataikirapo mtima.

Matimuwa akakumana lero ku Senegal, akuyembekezeka kubwerezana lachiwiri likubwerali pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.

M’masewero a mu gulu lomweli, usiku wapitawu Burkina Faso yababada Burundi 4-1.

Related posts

VisionFund Malawi donates K3 Million to support upcoming Lakeshore Conference

By Suleman Chitera

Galatasaray tried to sign Arsenal loan who only changed clubs in July

Malawi Freedom Network

Mpinganjira spoils Wanderers players

By Suleman Chitera

Family has played a huge role for Lakyle Samuel coming through at Manchester City

Malawi Freedom Network

Marc Bernal injury news

Malawi Freedom Network

The 6 best players in European football Gameweek 3 – ranked

Malawi Freedom Network

Leave a Comment

Leave a review

This website uses cookies to improve your experience. We'll assume you're ok with this, but you can opt-out if you wish. Accept Read More