Ulendo olowera ku Lower shire Wayambika

M’mawa wa lero lamulungu pa 1 December, 2024, His Excellency Prof Arthur Peter Mutharika ndi chipani chonse cha Democratic Progressive Party ( DPP) mchigawo chakummwera chikhala chikulowera Ku chigwa cha nsinje wa Shire.

Ulendowu wakonzedwa m’cholinga chokawadziwitsa anthu za kalembera wa mavote amene alinkati m’ma boma a Nsanje ndi Chikwawa kuphatikiza ma maboma ena monga Mangochi, Lilongwe komanso Mzimba.

Akulu-akulu a Chipani cha DPP, monga Mlembi Wamkulu Olemekezeka a Peter Mukhito, wachiwiri kwa mtsogoleri mchigawo chakummwera olemekezeka a Joseph Mwanamvekha MP, Mkulu okonza misonkhano m’chipani cha DPP olemekezeka a Sameer Suleman MP, Regional Governor Olemekezeka a Charles Mchacha MP komanso aphungu ndi ma khansala mchigawochi ndi amene akuyembekezeka kukalankhula m’malo onse amene mwakonzedwa misonkhano.

Related Posts

Mutharika Blocks CDF Amendment, Citing Weak Oversight and Risk of Abuse

By Suleman Chitera State House has confirmed that President Peter Mutharika has withheld assent to the Constitution (Amendment) Bill of 2025, delivering a sharp rebuke to Parliament over what the…

Print & Cut Steps Forward to Restore Iconic Mangochi Sign

By Suleman Chitera Print & Cut Company has reaffirmed its commitment to community pride and place branding, expressing strong optimism that the Mangochi District Council will approve its proposal to…

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

//otieu.com/4/9370459