Ulendo olowera ku Lower shire Wayambika

FB IMG 1733287665233

M’mawa wa lero lamulungu pa 1 December, 2024, His Excellency Prof Arthur Peter Mutharika ndi chipani chonse cha Democratic Progressive Party ( DPP) mchigawo chakummwera chikhala chikulowera Ku chigwa cha nsinje wa Shire.

Ulendowu wakonzedwa m’cholinga chokawadziwitsa anthu za kalembera wa mavote amene alinkati m’ma boma a Nsanje ndi Chikwawa kuphatikiza ma maboma ena monga Mangochi, Lilongwe komanso Mzimba.

Akulu-akulu a Chipani cha DPP, monga Mlembi Wamkulu Olemekezeka a Peter Mukhito, wachiwiri kwa mtsogoleri mchigawo chakummwera olemekezeka a Joseph Mwanamvekha MP, Mkulu okonza misonkhano m’chipani cha DPP olemekezeka a Sameer Suleman MP, Regional Governor Olemekezeka a Charles Mchacha MP komanso aphungu ndi ma khansala mchigawochi ndi amene akuyembekezeka kukalankhula m’malo onse amene mwakonzedwa misonkhano.

See also  Tensions Rise as Chakwera Disrupts Mutharika's Planned Visit to Mangochi Hospital

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *