DPP imangodziwa kunamiza A Malawi”- watero Kabwira

Chipani cha MCP chati chipani cha DPP ndichipani chabodza lotheratu chomwe chimangodziwa kunamiza a Malawi.

Izi zanenedwa kutsatira zomwe zayankhulidwa pamsonkhano wandale la Mulungu kwa Phwetekere mu mzinda wa Lilongwe ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP chigawo chapakati Alfred Gangata kuti misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP ndipo MCP ikungomalizitsa chabe.

FB IMG 1733759855451

misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP watero Gangata

Mneneli wachipani cha MCP Jessie Kabwira wauza Nkhoma Synod Radio kuti chipani cha DPP chilibe mfundo zogwilika ndipo Gangata ndi munthu yemwe amangoyankhula poti dziko lino lili ndi ufulu wademokalase koma simunthu omutengera zoyankhula zake.

Malingana ndi a Kabwira misewu yonse yomwe ikumangidwa padakali pano mwini wake ndi MCP osati zomwe akunena a Gangata kaamba koti DPP ndichipani chomwe chimangodziwa kuba osati kutukula dziko lino.

Related Posts

Step 30 International Ministries Brings Life-giving Water To Chingala Village

By Mabvuto Kalawa, Malawi Freedom Network Correspondent In a remarkable display of compassion and community development, Step 30 International Ministries has drilled a solar-powered borehole in Chingala Village, Lilongwe District,…

Redson Munlo Quits MCP, Cites Personal Decision Amid Growing Party Discontent

By Suleman Chitera Redson Munlo, a well-known political activist and member of the Malawi Congress Party (MCP), has resigned from the party, marking yet another high-profile exit at a time…

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

//otieu.com/4/9370459