FB IMG 1733759850573

Chipani cha MCP chati chipani cha DPP ndichipani chabodza lotheratu chomwe chimangodziwa kunamiza a Malawi.

Izi zanenedwa kutsatira zomwe zayankhulidwa pamsonkhano wandale la Mulungu kwa Phwetekere mu mzinda wa Lilongwe ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP chigawo chapakati Alfred Gangata kuti misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP ndipo MCP ikungomalizitsa chabe.

FB IMG 1733759855451

misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP watero Gangata

Mneneli wachipani cha MCP Jessie Kabwira wauza Nkhoma Synod Radio kuti chipani cha DPP chilibe mfundo zogwilika ndipo Gangata ndi munthu yemwe amangoyankhula poti dziko lino lili ndi ufulu wademokalase koma simunthu omutengera zoyankhula zake.

Malingana ndi a Kabwira misewu yonse yomwe ikumangidwa padakali pano mwini wake ndi MCP osati zomwe akunena a Gangata kaamba koti DPP ndichipani chomwe chimangodziwa kuba osati kutukula dziko lino.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Contact Us on WhatsApp