Chipani cha MCP chati chipani cha DPP ndichipani chabodza lotheratu chomwe chimangodziwa kunamiza a Malawi.
Izi zanenedwa kutsatira zomwe zayankhulidwa pamsonkhano wandale la Mulungu kwa Phwetekere mu mzinda wa Lilongwe ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP chigawo chapakati Alfred Gangata kuti misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP ndipo MCP ikungomalizitsa chabe.

misewu yamakono yomwe ikumangidwa mu mzinda wa Lilongwe inayambidwa ndi chipani cha DPP watero Gangata
Mneneli wachipani cha MCP Jessie Kabwira wauza Nkhoma Synod Radio kuti chipani cha DPP chilibe mfundo zogwilika ndipo Gangata ndi munthu yemwe amangoyankhula poti dziko lino lili ndi ufulu wademokalase koma simunthu omutengera zoyankhula zake.
Malingana ndi a Kabwira misewu yonse yomwe ikumangidwa padakali pano mwini wake ndi MCP osati zomwe akunena a Gangata kaamba koti DPP ndichipani chomwe chimangodziwa kuba osati kutukula dziko lino.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!
