Kusamvana komwe kunalipo m’chipani cha DPP pa yemwe akuyenera kukhala mkulu wa zipani zotsuta boma m’nyumba ya malamulo kwatha tsopano.
Izi zikutsatira m’gwirizano omwe mbali zokhuzidwa zapanga kuti a Kondwani Nankhumwa akhalebe pampandowu.
Malingana ndi mneneri wa chipani cha DPP, Shadrec Namalomba, a Nankhumwa akhalabe pa udindowu kufikira pomwe chipanichi chidzachititsenso chisankho china cha mtsogoleri wa zipani zotsutsa m’nyumbayi.
“Tinafunsa bwalo la milandu kuti litipatse nthawi yomwe tingakhale titachitanso chisankhochi, koma wodandawula anakana kuti izi zisakhudzee bwalo la milandu,” yatero kalata yomwe a Namalomba atulutsa.
Read also: Mulhakho wa Alhomwe Cultural Festival excludes MCP from invitations
Read also: Ben Longwe advises Chihana to take plus one vote to the South
Read also: Mulhako wa Alhomwe 2026 Targets K300 Million
Ganizoli ladza kutsatira zokambirana zomwe zachitika ndipo mkhala pakati wake anali oweluza milandu, Kenyatta Nyirenda.
Kusamvanaku kunadza, pomwe aphungu ena a DPP anasankha a George Chaponda kukhala pa udindowu pa mkumano wawo wina ku nyumba ya mtsogoleri wa chipanichi, Peter Mutharika ku Mangochi.
Aphungu ena sadakondwe ndi izi ndipo anakamang’ala ku bwalo la milandu.
Mbali ya a Chaponda akuti yavomerezanso kuti inalakwitsa kuwasankha pa mpandowu popanda aphungu ena.
Read also: Chakwera Given Seven Days To Fire Martha Chizuma
Read also: Sulom unpacks revised prizes
Read also: Lightning kills two in Lumbadzi





