ANTHU AYAMBA KUPALA WOKHA MISEWU

Atatopa ndikudikira kuti boma komanso andale awakonzere msewu olumikiza maboma a Dedza ndi Salima kudzera ku dera la Kasumbu, anthu okhala m’madera a Mfumu Madzumbi Nakaona, Chiwamba ,Ndembo ndi nzoola m’dela la Mfumu yayikulu Kasumbu ku Dedza akupala okha ndi makasu msewu wotalika makilomita 12 omwe ndioipa kwambiri.

A Gulupu a Madzumbi atiuza kuti anaganiza zochita izi kaamba kakuti kwanthawi yaitali akhala akuvutika kwambiri popita ku msika kukagulitsa mbewu, komanso kukapeza zofunikira pa moyo wawo watsiku ndi tsiku.

Iwo atinso chifukwa china nchakuti msewu akupalawu ndi wachidule kuyerekeza ndikuzungulira ku boma la Dedza koyenda ma ola 9.

Mafumu ndi anthu kumeneko apempha akulu akulu kuti asiye kuwakumbukira nthawi ya chisankho yokha komanso kuthana mavuto omwe akukumana nawo.

Related Posts

DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window