Sat. Apr 20th, 2024

CHAKWERA NDI CHILIMA ANAPANGA MGWILIZANO OTI AZALAMULIRA ZAKA ZIWILI NDI MIYEZI 6 WINA ALIYESE

By Suleman Chitera Apr27,2022

BREAKING NEWS; CHAKWERA NDI CHILIMA ANAPANGA MGWILIZANO OTI AZALAMULIRA ZAKA ZIWILI NDI MIYEZI 6 WINA ALIYESE

Mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera ndi mlembi wachipani cha MCP Eisenhower Mkaka zulo anakhumudwisa akuluakulu ena achipani cha MCP atatulusa poyela mfundo zomwe Dr Lazarus Chakwera ndi Dr Saulos Chilima anagwilizana mene ankatenga boma muchaka cha 2019.

Awiliwa abwela poyela kamba koti Dr Saulos Chilima akuwonesa kuti sopano wayamba zamatukutuku pokonzekela kuzatenga boma kumathelo a mwezi wa December chaka chino kapena pa 1 January chaka cha 2023

Chakwera anati zipani za MCP ndi UTM zisanatenge boma zinayamba kukambilana mfundo yoti Dr Lazarus Chakwera azalamulile zaka kenako Dr Saulos Chilima nawo azalamulile zaka zina 5 mwatsoka chipani cha UTM chinakanisisa ponena kuti ndizinthu zakutali ndipo zamoyo siziziwika.

Chakwera anapitiliza kunena kuti zokambilana zoyamba zitalepheleka mbali ziwilizi zinagwilizana mfundo yoti iye azalamulile zaka ziwili ndimiyezi 6 kenako azasiyile Dr Saulos Chilima nawo kuti azalamulile zaka zina ziwili ndimiyezi 6 koma munthawiyo Vice President azachokela kuchipani cha MCP ndipo azakhala mlembi wachipanicho omwe ndi Eisenhower Mkaka.

Popitiliza nkhaniyi a Eisenhower Mkaka anawuza akuluakulu achipani cha MCP kuti mbali ziwilizi zitagwilizana mfundo yolamulira zaka ziwili ndi miyezi 6, anayitanisa ma Lawyer ndima Judge ena omwe anazasayinila panganoli.

“Bwanji simunatiwuze nthawi yonseyi” “eti..eti…inu” akuluakulu ena achipani cha MCP anamveka kung’ona chapansipansi zomwe zinachitisa.

Zokambila zinafika povuta kamba koti ma membala ena samagwilizana ndipanganoli ndipo amunisisa kuti Dr Lazarus Chakwera akathese mgwilizanowo

Anthuwa atelephela kumvana Dr Chakwera anayimisa kaye zokambilana kufikila sabata yamawa pomwe azagwilizane mfundo zingapo za nkhaniyi ndi nkhani zina.

Pakanali pano Dr Saulos Chilima wayamba kale kugula magalimoto ochuluka muchipani chake kamba akuziwa zoti kunja kwamuchela ndipo nthawi.

Related Posts
DPP Blues Rebels Brings Division In
DPP Blues Rebels Brings Division In

The way Charles Mchacha is castigating the Leader of Opposition in Parliament, Hon Kondwani Nankhumwa, is just testimony enough that Read more

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Malawi Government Faulted Over Arrests of Coup Suspects

The recent arrest in Malawi of three opposition politicians accused of planning to unseat President Peter Mutharika is dissent from Read more

Allegations of a coup plot sour diplomatic ties

The US embassy has denied involvement in an alleged plot to overthrow the president, Peter Mutharika. Analysis Media reports that Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

President Lazarus Chakwera has officially opened the Blantyre International Cancer Centre, The private health facility, has been constructed by the Thomson and Barbara Mpinganjira Foundation