Wapambando wa bungwe la Muslim Association of Malawi (MAM) Sheikh Idrisa Muhammad akuti chilengezereni a FDH Bank masiku atatu apitawa, kuti akhazikitsa Islamic Banking mdziko muno, iwo ngati bungwe la MAM akulandira pempho kuchokera ku ma bank ena mdziko muno kuti nawo ayambise Islamic Banking.
Iwo ati izi ndi zomwe amayembekezera, ndipo akufunisitsa ikamafika miyezi inayi asilamu ochuluka akhale ayamba kusungisa ndalama zawo ku FDH Salama Banking Solution.
Mtsogoleriyu wapempha asilamu onse mdziko muno kuti akatsegulise mwansangansanga ma account awo ndi FDH SALAMA BANKING SOLUTION.
Sheikh Idrisa Muhammad ayankhula izi mmawa wa lero ku Mudi ku Limbe ku ma ofesi a Darusunnah Foundation komwe bungwe la Darusunnah Foundation lakhala bungwe loyambilira kutsegulira ma account ku FDH Salama Banking Solution kwa ana amasiye omwe bungweli limawathandiza.
Ndalama zokwana 35 miliyoni kwacha ndi zomwe bungwe la Darusunnah Foundation layika ku FDH Salama Banking Solution ndipo ana amasiye okwanira 74 ochokera mmaboma osiyanasiyana mdziko muno ndi omwe alandira ndalamazi.
Abdul Rahman Chowe yemwe ali Mlembi wankulu wa Darusunnah Foundation wati bungweli lafuna kukhala lachitsanzo chabwino popereka sapoti ku FDH Salama Banking Solution ndi cholinga mabungwe ena achisilamu nawonso atatero.