Chipani cha DPP chati chikubweleraso m’boma chaka cha mawa kuti chiwombole anthu pa mavuto.
Mkulu owona zokopa anthu m’chipanichi a Everton Chimulirenji ayankhula izi la mulungu pa msonkhano omwe chipanichi chinachititsa ku Ntcheu.
A Chimulirenji ati a Malawi akudutsa mu nyengo zowawa kuphatikizapo njala ndi kukwera mitengo kwa zinthu.
Iwo ati chipanichi chakonzeka kuwaombola a Malawi pa mavutowa kaamba koti mayankho a Malawi ali ndi chipanichi.
Pa msonkhanowu, chipanichi chinalandiraso m’modzi mwa anthu omwe awonetsa chidwi chodzaimira pa mpando wa phungu wa chipanichi m’bomali a Mandela Ndilinde Gomeza.