Ine ndikuti gabadinho Akufunika ku flames – watero Mvula
Katswiri pa nkhani za masewero a Humphreys Mvula wati sakugwirizanabe ndi mphunzitsi wamkulu watimu ya Flames Patrick Mabedi pomamusiya Gabadinho Mhango mumasewero ake osiyanasiyana pomati wakula.
A Mvula ati Mabedi akuyenera kuganizira bwino pa za osewera wa Marumo Gallants-yu pomwe iwo akuti sakukhulupilira zoti Mhango anatha kuti sangatumikire timu yadziko lino.
Read also: Mzuzu small-scale business operators meet with president Chakwera
Read also: Aford’s Enock Chihana Promises K5 Billion Development Boost Per Constituency if Mutharika Wins
Read also: US Election 2024 Analysis: A Deadlocked Race and the Final Push for Victory
A Mvula ati timu yadziko lino ikufunika kuyimanga ndi osewera omwe ndi akuluakulu komanso ena achisodzera pofuna kuti awa obwera kumene adziphunzira kwa akalewa.
Mphunzitsi Mabedi sabata yatha anawuza olemba nkhani kuti iye alibe zotsamwitsa zili zonse ndi Mhango posamutenga mumasewero atimuyi ndi Burundi komanso Burkina Faso mumpikisano ofuna kudzipezera malo kundime yotsiliza ya Africa Cup of Nations.
Read also: A legacy of lies: A damning analysis of President Chakwera’s State of the Nation Address
Read also: 29-Year-Old Arrested for Allegedly Stealing Cattle Worth K7 Million in Chikwawa
Read also: FDH Bank Cup 2025: Nyasa Big Bullets and Mighty Wanderers on Course for Semi-Final Clash





