Katswiri pa nkhani za masewero a Humphreys Mvula wati sakugwirizanabe ndi mphunzitsi wamkulu watimu ya Flames Patrick Mabedi pomamusiya Gabadinho Mhango mumasewero ake osiyanasiyana pomati wakula.
A Mvula ati Mabedi akuyenera kuganizira bwino pa za osewera wa Marumo Gallants-yu pomwe iwo akuti sakukhulupilira zoti Mhango anatha kuti sangatumikire timu yadziko lino.
A Mvula ati timu yadziko lino ikufunika kuyimanga ndi osewera omwe ndi akuluakulu komanso ena achisodzera pofuna kuti awa obwera kumene adziphunzira kwa akalewa.
Mphunzitsi Mabedi sabata yatha anawuza olemba nkhani kuti iye alibe zotsamwitsa zili zonse ndi Mhango posamutenga mumasewero atimuyi ndi Burundi komanso Burkina Faso mumpikisano ofuna kudzipezera malo kundime yotsiliza ya Africa Cup of Nations.
MALAWI
FREEDOM
NETWORK
United for Freedom, Justice and a Better Malawi
Airtel Money
0994095804
Mpamba
0881428759
FDH Bank
Acc No:
1400000670385NBS Bank
Acc No:
10118988Thank you for your support!