FB IMG 1725821570372

Mphunzitsi wa timu ya mpira wamiyendo ya dziko lino ya Flames, Patrick Mabedi, wati mwa njira ina ili yonse, timuyi ikuyenera kupeza chipambano pamasewero ake ndi Burkina Faso lachiwiri likudzali ku Bamako dziko la Mali.

Mabedi walankhula izi atangofika m’dziko la Mali komwe anyamata ake awongola minyewa komanso kuchita zokonzekera zoyamba za masewerowa, kuti timuyi idzigulire malo mu mpikisano wa Africa Cup of Nations (AFCON).

Mphunzitsiyu wati sakuyenera kumataya ma pointi kuti akhale ndi mwayi waukulu ochita bwino, potengera kuti ma timu ena m’gululi Senegal komanso Burkina Faso anafanana mphamvu pamasewero awo.

Mabedi, yemwenso ndi katswiri wakale otchinga kumbuyo mu timu ya Flames, walongosolanso kuti anali ndi nthawi younika zolakwika zomwe anyamata ake anachita pamasewero omwe anagonja 3-2 ndi Burundi, ndipo akuyembekeza chipambano pa masewerowa.

Ndipo, timu ya Burundi yomwe ili mugulu L yaitanitsa anyamata a Senegal mawa, lolemba, pa bwalo la Bingu nzinda wa Lilongwe.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

See also  “This is our moment to reclaim Malawi’s destiny,” says Mutharika

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *