Nduna yofalitsa nkhani yemwenso ndi mneneri waboma Moses Kumkuyu wati zomwe wayankhula mtsogoleri wachipani cha UTM dzulo pamsonkhano wa atolankhani zikuonetselatu kuti sadziwa momwe boma limayendera.

Dzulo a Kabambe anadzudzula mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera ponena kuti akungokhalira kupempha thandizo mmaiko akunja zomwe akuti wasandutsa a Malawi ambiri kukhala ‘a Lazalo opemphapempha’.

Komatu mneneri wabomayu wati a Kabambe angowonetselatu kuti ndi munthu yemwe sakudziwa momwe kayendetsedwe kaboma kamakhalira.

“Zomwe ayankhula abambo amene aja sizoona. Dziko lino lili mugulu la maiko osaukitsitsa ndipo kuti titulukemo tikuyenera ndithu kuti anzathu atigwire dzanja.

“Komansotu sichanzeru kuti mtsogoleri azilephera kupempha thandizo pomwe anthu mdziko lake akufa ndi njala ati poopa kuti anthu amuseka kuti akupempha kwambiri. Limenelo ndi thamo. Tsono mtsogoleri asamakhale wathamo.” Watelo Kumkuyu.

Mwazina a Kabambe anati iwo akadzalowa m’boma chaka chamawa adzaonetsetsa kuti akuika ndalama kuntchito yotukula dziko lino ndipo azidzalolera kuyenda wapansi bola ntchito zachitukuko zikupita patsogolo.

Sponsored • Malawi Freedom Network

MALAWI
FREEDOM
NETWORK

United for Freedom, Justice and a Better Malawi

Airtel Money

0994095804

Mpamba

0881428759

BANK TRANSFER

FDH Bank

Acc No:

1400000670385

NBS Bank

Acc No:

10118988

Thank you for your support!

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *