
Silver Strikers Yagonjesa Premier Bet Dedza Dynamos
Timu ya Silver Strikers yapereka ubatizo wa zigoli ku timu ya Premier Bet Dedza Dynamos mu mpikisano wa Airtel Top 8 pa bwalo la Silver mu nzinda wa Lilongwe.
Anayambitsa zonse anali Chimwemwe Idana ndipo Zebron Kalima anamwetsanso chimodzi asanabwere Chinsinsi Maonga kudzayedzeka zake ziwiri.
Ndipo Chifuniro Mpinganjira anamwetsa Chigoli chokhacho cha timu ya Dedza Dynamos.
Atatha masewerowa Mphunzitsi wamkulu Wa Silver Strikers, Peter Mponda, wati ndiokhutira ndi kupambanaku komanso momwe osewera ake anachitira.
”Anyamata anamva zomwe tinakambirana tisanabwere mu masewerowa ndipo ndiyamikire kuti achita bwino pochinya zigoli zambiri komanso kusewera bwino,” watero Mponda.
Read also: MBC district reporters obtains court injunction
Read also: Malawi Elections 2025: Peter Mutharika Takes Strong Lead With 71.2% of Votes Counted
Read also: Ayuba James accepts IPOR survey on Mutharika’s lead
M’mau ake Mphunzitsi wamkulu wa Premier Bet Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati sizinayende momwe anakonzekera chifukwa anachinyitsa m’sanga komanso chigoli chachiwiri chomwe ndichokaikitsa chinasokoneza osewera ake.
‘Tagonja koma sikuti tathera pamenepa tikayesesa masewero a chibwereza kukachinya komanso kuteteza bwino kuti tikathe kufika ndime ina,” watero Bunya.
Kalima ndiye anasankhidwa kukhala dolo mbambande kuposa onse mumasewerowa.
Masewero a chibwereza alipo pa 20 October pa bwalo la Dedza.
Read also: Ine ndikuti gabadinho Akufunika ku flames – watero Mvula
Read also: No More General January! Get Your Akasi Sausage Today!
Read also: Mhango Orders Crackdown on Driving Schools as Road Deaths Spiral



















