
Civil Service United ndi MAFCO FC alepherana posagoletsana
Ma timu a Civil Service United ndi MAFCO FC alepherana posagoletsana chigoli chili chonse ngati zopangana pamasewero omwe analipo masanawa pa bwalo la Civo mu ligi ya TNM.
Poyankhula atatha masewerowa, wachiwiri kwa mphunzitsi ku Civil, Wilson Chidati, wamvomereza kuti mpira unawavuta kamba koti chili chonse chomwe anakonzekera sichinatheke pamasewerowa.

Kumbali yake, wachiwiri kwa mphunzitsi ku timu ya Mafco, Jimmy Mzunga, wati anabwera ngakhale abwera kuti adzapambene, komabe walimbikitsa osewera ake kuti masewero otsatira adzachite bwino.
Read also: Walter Nyamilandu Vows to Transform Nsanje South West if Elected MP
Read also: Controversial Martha Chizuma Leaked Audio That Led Her To Interdiction
Read also: My simple advice to Bakili Muluzi TV
Timu ya Civil yafika pa nambala 5 itasewera masewero 20 ndipo ili ndi mapointi 28 pamene Mafco ili pa nambala 8 pamasewero 20 ndipo ali ndi 27.
Christopher Gototo ndi yemwe anasankhidwa kuti wasewera bwino kuposa osewera onse pamasewerowa.
Read also: Dalitso Kabambe ndi Yankho Lathu la 2030: “Sitifunanso Kulakwisanso,” Atero Amalawi
Read also: LSF Opens New Hospital In Lilongwe
Read also: Mutharika showers Blantyre Synod pastors with cash and promises



















