Mphuzitsi wa timu ya mpira wamiyendo yadziko lino Patrick Mabedi wati tsopano agwilitsa ntchito masewela omwe atsala odzigulira malo mumpikisano wa Afcon ngati mbali yokozekela masewera odzigulira malo mumpikisano wapadziko lonse a World Cup.
A Mabedi ayankhula izi kutsatira pomwe timuyi yalephera kudzigulira malo mu mipikisano wa AFCON kutsatila kugonja ndi team ya Senegal 1-0 pamasewero omwe anachitika lero pabwalo la zamasewero la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.
Read also: Bishop Stima encourages spiritual transformation
Read also: Electricity To Go Up
Read also: Al- Barakah Charity Trust Donates To Cyclone Freddy Survivors
Malingana ndi a Mabedi ati timu yadziko linoyi siikuchita bwino kaamba kosakozekera bwino kotero masewero omwe atsalawa apeleka danga lokoza pomwe pakumavunda khola cholinga choti timuyi iyambe kuchita bwino.
Pakadali pano Flames ili pansi penipeni pa gulu L ndipo ilibe ngakhale point ndiimodzi yomwe kuchoka mumasewero anayi omwe yasewera.
Read also: Sugar Is Available On The Market.
Read also: Kalindo urges politicians to reflect on Chilembwe Day preaching
Read also: Family Refused To Collect Dead Body of Relative From Queen Elizabeth Central





