Timu ya Dedza Dynamos FC tsopano izitchedwa Premier Bet Dedza Dynamos FC kutsatira thandizo la ndalama zokwana K100 million zomwe kampaniyi yapereka lero.
Mgwirizanowu ndi wa chaka chimodzi ndipo mkulu wa Premier Bet, a Trevor Whitaker wati akuyembekezera zotsatira zabwino ku timuyi mu ligi ya TNM.
Mmawu ake, mkulu wa timuyi a Hastings Mpanbira wati apweteka matimu chaka chino.
Naye mtsogoleri wa Football Association of Malawi {Fam} a Fleetwood Haiya wayamikira kampani ya Premier Bet kamba ka thandizoli pomwe wati izi zibweretsa mangolomera ku timuyi komanso kampani zina.
Premier Bet iziperekanso ndalama zokwana 100 thousand kwacha kwacha kwa wosewera mmodzi wapamwamba mwezi uli onse, 500 thousand kwacha kwa osewera mbambande pamapeto a ligi komanso 200 thousand kwacha kwa ochemelera wapamwamba ku timuyi.