Wochita malonda Triephornia Mpinganjira walengeza kuti athandiza ndi K18 million achinyamata omwe akufuna kuchita malonda koma alibe kuthekera.
A Mpinganjira alengeza izi pa tsamba lawo la Facebook, ndipo ati iyi ikhala ndalama yothandiza achinyamatawo kuti apeze poyambira.
Kudzera mu ndondomekoyi, wachinyamata aliyense alandira K1 million atapereka pulani yabwino ya malonda omwe akufuna kuchita..
Malinga ndi a Mpinganjira, ndalama yokwana K1 million idzipelekedwa kwa m’nyamata m’modzi pa sabata ziwiri ndipo izi zikhala zikuchitika mpaka mwezi wa December chaka chino.
Achinyamata a zaka za pakati pa 18 ndi 35 ndi omwe akuyenera kutenga nawo gawo pa ndondomeko yomwe akuitcha: “Kuthandiza omwe alibe kuthekela kupita patsogolo”.