Tue. Apr 23rd, 2024

Phungu Apempha Boma Kuti Lilole Anthu Aziweta Nyama Ya Pangolin

Akuluakulu ku nthambi yoona za chilengedwe ati nzosatheka kuti dziko la Malawi liloleze anthu kuyamba kuweta Ngaka (Pangolin).

Brighton Kumchedwa, nkulu woona za malo osungirako nyama ndi zachilengedwe zina wanena izi lero kunyumba ya malamulo, pomwe amayankha funso lochoka kwa phungu wa dera la Chiradzulu East Joseph Nomale yemwe anadabwa kuti nchifukwa chani boma likumanga anthu omwe akupezeka ndi Ngaka mmalo mosiya kuti anthu adziweta ndikumagulitsa.

Nomale adati Ngaka ikufunidwa ndi maiko ambiri ndipo ogula akumagula nyamayi ndi ndalama yakunja ya Dollar, zomwe zingapindulire dziko la Malawi ngati ataloleza kuti anthu adziweta mmakomo mwawo.

Malingana ndi Nomale, nzodabwitsanso kuti aboma akuti Ngaka ndi nyama yotetezedwa chonsecho nyamayi ikumapezeka ikungoyenda mminda mwa anthu.

Koma Kumchedwa wati zomwe a Nomale akunena nzosatheka chifukwa Ngaka ndi nyama yotetezedwa pa malamulo a dziko lino Komanso malamulo ena a dziko lonse lapansi omwe anaika nyamayi pa ndandanda wa nyama zomwe moyo wake uli pa chiopsezo.

Kumchedwa watinso nzosatheka kuweta Ngaka pakhomo chifukwa choti si nyama yoti munthu utha kumadyetsera.

“Ena akaba Pangolin amapezeka akuikakamiza nyamayi kuti idye nsima, izi zamapeleka chiopsezo ku moyo wake ndipo itha kufa. Izi zikusonyeza kuti Pangolin si nyama yoti utha kuweta pakhomo chifukwa imazisakira yokha zakudya ngati nyerere zomwenso zimapezeka kwambiri nkhalango ndi malo ena”, adatero Kumchedwa.

Pakadali pano Werani Chilenga wapampando wa komiti yoona zachilengedwe wauza anthu kuti atalikirane ndi nyamayi ponena kuti aliyense opezeka nayo akalowa kundende.

Related Posts
Mumba Should Clear Himself On The Alledged Corrupt Dealings Alongside Chinese Companies

Alot has been said regarding corrupt undertakings by one Engineer Vitumbiko Mumba who is on a mission to enrich himself Read more

ROADS AUTHORITY WARNED NOT TO HIRE INEXPERIENCED ENGINEER AS CEO

Hiring of a new Chief Executive Officer at Roads Authority has been thrown into bad light because some of the Read more

Exposed! HTD boss Abdul Aboobaker corruptly, illegally bought land building Mug & Bean in Lilongwe

MUG AND BEAN: Abdul Majid Aboobaker corruptly acquired this plot and has since been closed Details have emerged how HTD Read more

Corrupt Asian businessman Abdul Karim Batatawala captures Chakwera’s State House

BATAWALALA: He has captured state houseAsian ‘corrupt’ businessman Abdul Karim Batatawala of the infamous Immigration Department ‘Uniform Scandal’ is reportedly Read more

Other stories

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

Ekhaya luxury Resort fully open