Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemweweso ndi mtsogoleri wachipani chotsutsa boma cha Democratic Progressive -DPP Prof. Peter Munthalika wadzudzura boma la Dr. Lazarus Chakwera ati kamba kolephera kuyendetsa bwino dziko lino.
A Munthalika amalankhura izi masanawa pa msonkhano wa atolankhani omwe umachitikira kunyumba kwawo ku Mangochi.
Iwo ati ndizomvetsa chisoni kuti aMalawi akulephera kupeza zinthu zofunikira monga ziphaso zoyendera (passports)komaso ziphaso zoyendetsera galimoto.
Iwo ati ngakhale mavutowa alipo m’dziko muno aMalawi asadandaule ndipo asadere nkhawa chifukwa chipani chawo chakonzeka kudzamuliraso dziko lino akasankhidwa pa chisankho cha chaka chamawa.