Atatu ali mmanja mwa apolisi kamba kopha munthu

Anthu atatu anjatidwa kamba kowaganizila kuti apha a Charles Assan azaka 32 omwe amagwira ku Bank ya First Capita Bank m’boma la Dowa.

Mneneri wa Polisi ku Mponera a Macpatson Msadala ati atatuwa ndi a Jafali Mtungwe emwe ndi dalaivala wa Bungwe la NEEF , Nelson Jossam ndi chibwenzi chake Halima Kamwana.

Nkhaniyi ikuti Malemuwa ndi anthu ena awiri a Nelson Jossam ndi a Halima Kamwana atamaliza kumwa mowa pa Malo ena a Sunrise anakonza zomapita kwawo koma sanapeze Taxi iliyonse yoti iwatenge.

Ali mofufuzabe Taxi-yi iwo anaona Galimoto ina ya Toyota Hilux Pickup yomwe inali ya bungwe la NEEF ndipo imaendetsedwa ndi a Jafali Mtungwe ndipo atapepha anawaloledza kuwatenga kuti akawasiye ku dera la Nkhamanga.

Ali mu Galimotoli anasephana maganizo zomwe zinapangitsa kuti dalaivalayi awatulusemo ndipo atatulukamo woyendetsayi anayendetsa Galimoto yomwe inagunda Malemuwa.

Chipatala Chamadisi Mission chapedza kuti a Assan amwalira kamba kovuladzidwa pogundidwa komanso thupi lawo lapezeka ndimabala olumidwa.

Related Posts

Malawi Freedom Network advice President Banda to fight corruption

If you thought Malawians are lazy people, I bet you a Dinosaur, think twice and you will know, check in Read more

Mustag Chothia, Sulema Ismael Karim In Land scam

Land remains one area that Malawians know has been heavily abused, characterised by ownership wrangles, not to mention corruption, fueled Read more

Kalindo Wapempha Chakwera Achotse Ntchito Chizuma Masiku Okwana Asanu Ndi Awiri

Mkulu wa bungwe la Concerned Citizens and Timely Voices (CCTV) Bon Kalindo, wapempha mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera Read more

The Concerned Citizens Furious With Chizuma’s Stubbornness

The concerned citizens group which is advocating for sanity in civil service have vowed to take drastic measures in responding Read more

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *

FDH Launch Islamic Banking Window